Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 10:17-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo anapsa mtima pa Eleazara ndi Itamara, ana otsalawo a Aroni, nati, Mwalekeranji kudya nsembe yaucimo m'malo opatulika, pakuti ndiyo yopatulikitsa, ndipo iye anakupatsani iyo, kucotsera nayo mphulupulu ya khamulo, kuwacitira cowatetezera pamaso pa Yehova?

18. Taonani, sanalowa nao mwazi wace m'malo opatulika m'katimo; mukadaidyera ndithu m'malo opatulika, monga ndinakuuzani.

19. Ndipo Aroni analankhula ndi Mose, nati, Taonani, lero abwera nayo nsembe yao yaucimo ndi nsembe yao yopsereza pamaso pa Yehova; ndipo zandigwera zotere; ndikadadya nsembe yaucimo lero, kukadakomera kodi pamaso pa Yehova?

Werengani mutu wathunthu Levitiko 10