Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 9:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Kunena za Efraimu, ulemerero wao udzauluka ndi kucoka ngati mbalame; sipadzakhala kubala, ndi kukhala ndi pakati, ndi kuima.

12. Angakhale alera ana ao, koma ndidzawasowetsa, wosatsala munthu; ndithunso tsoka iwowa, pamene ndiwacokera.

13. Efraimu, monga ndaona, akunga Turo, wookedwa pokoma; koma Efraimu adzaturutsira ana ace wakuwaphera.

14. Apatseni, Yehova; mudzapatsa ciani? muwapatse mimba yotayataya, ndi mawere ouma.

15. Coipa cao conse ciri m'Giligala; pakutipamenepo ndinawada, cifukwa ca kuipa kwa macitidwe ao ndidzawainga kuwacotsa m'nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.

16. Efraimu wakanthidwa, muzu wao wauma, iwo sadzabala zipatso; inde ngakhale abala, koma ndidzapha zipatso zofunika za mimba yao.

17. Mulungu wanga adzawataya, pakuti sanammvera Iye; ndipo adzakhala othawathawa mwa amitundu.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 9