Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 9:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usakondwera, Israyeli, ndi kusekerera, ngati mitundu ya anthu; pakuti wacita cigololo kuleka Mulungu wako, wakonda mphotho ya cigololo pa dwale la tirigu liri lonse.

2. Dwale ndi coponderamo mphesa sizidzawadyetsa, vinyo watsopano adzamsowa.

3. Sadzakhala m'dziko la Yehova; koma Efraimu adza bwerera kumka ku Aigupto; ndipo adzadya cakudya codetsa m'Asuri.

4. Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa acisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m'nyumbaya Yehova.

5. Mudzacitanji tsiku la masonkhano oikika, ndi tsiku la madyerero a Yehova?

6. Pakuti taonani, anacokera cionongeko, koma Aigupto adzawasonkhanitsa, Mofi adzawaika m'manda; khwisa adzalanda zofunika zao zasiliva; minga idzakhala m'mahema mwao.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 9