Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 7:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukila zoipa zao zonse; tsopano macitidwe ao awazinga; ali pamaso panga,

3. Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.

4. Acigololo onsewo; akunga ng'anjo anaitenthetsa wooca mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.

5. Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lace pamodzi ndi oseka.

6. Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng'anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wooca mkate wao agona usiku wonse, m'mawa iyaka ngati moto wa malawi.

7. Onsewo atentha ngati ng'anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.

8. Efraimu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efraimu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 7