Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 7:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Efraimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Aigupto, amuka kwa Asuri.

12. Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m'mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.

13. Tsoka kwa iwowa! pakuti anandizembera; cionongeko kwa iwowa! pakuti anandilakwira; ndikadawalanditsa Ine, koma anandinenera zabodza.

14. Ndipo sanapfuulira kwa Ine ndi mtima wao, koma alira pakama pao, asonkhanira tirigu ndi vinyo, apikisana ndi Ine.

15. Cinkana ndawalangiza ndi kulimbitsa manja ao, andilingiririra coipa,

Werengani mutu wathunthu Hoseya 7