Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 7:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. M'mene ndiciritsa Israyeli, mphulupulu ya Efraimu ibvumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti acita bodza, ndipo mkhungu alowa m'nyumba, ndi gulu la mbala manca kubwalo.

2. Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukila zoipa zao zonse; tsopano macitidwe ao awazinga; ali pamaso panga,

3. Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.

4. Acigololo onsewo; akunga ng'anjo anaitenthetsa wooca mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.

5. Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lace pamodzi ndi oseka.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 7