Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 4:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma munthu asatsutsane ndi mnzace, kapena kudzudzula mnzace; popeza anthu ako ndiwo akunga otsutsana ndi wansembe.

5. Ndipo udzakhumudwa usana, ndi mneneri yemwe adzakhumudwa pamodzi ndi iwe usiku; ndipo ndidzaononga mai wako.

6. Anthu anga aonongeka cifukwa ca kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala cilamulo ca Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.

7. Monga anacuruka, momwemo anandicimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.

8. Adyerera cimo la anthu anga, nakhumbira cosalungama cao, yense ndi mtima wace.

9. Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga cifukwa canjira zao, ndi kuwabwezera macitidwe ao.

10. Ndipo adzadya, koma osakhuta; adzacita cigololo, koma osacuruka; pakuti waleka kusamalira Yehova.

11. Cigololo, ndi vinyo, ndi vinyo watsopano, zicotsa mtima,

12. Anthu anga afunsira ku mtengo wao, ndi ndodo yao iwafotokozera; pakuti mzimu wacigololo wawalakwitsa, ndipo acita cigololo kucokera Mulungu wao.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 4