Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 3:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova anati kwa ine, Mukanso, konda mkazi wokondedwa ndi bwenzi lace, koma wakucita cigololo monga Yehova akonda ana a Israyeli, angakhale atembenukira ku milungu yina, nakonda ncinci za mphesa zouma.

2. M'mwemo ndinadzigulira iye ndi ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndi homeri ndi nusu wa barele;

3. ndipo ndinati kwa iye, Uzikhala ndi ine masiku ambiri, usacita cigololo, usakhala mkazi wa mwamuna ali yense; momwemo inenso nawe.

4. Pakuti ana Israyeli adzakhala masiku ambiri a opanda mfumu, ndi opanda kalonga, ndi opanda nsembe, ndi opanda coimiritsa, ndi opanda efodi kapena aterafi;

Werengani mutu wathunthu Hoseya 3