Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 13:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Iri kuti mfumu yako tsopano, kuti ikupulumutse m'midzi yako yonse? ndi oweruza ako amene unanena za iwo, Ndipatseni mfumu ndi akalonga?

11. Ndinakupatsa mfumu mu mkwiyo wanga; ndinamcotsanso m'ukali wanga.

12. Mphulupulu ya Efraimu yamangika, cimo lace lisungika.

13. Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asacedwe mobalira ana.

14. Ndidzawaombola ku, mphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako iri kuti? manda, cionongeko cako ciri kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.

15. Cinkana abala mwa abale ace, mphepo ya kum'mawa idzafika, mphepo ya Yehova yokwera kucokera kucipululu; ndi gwero lace lidzaphwa, ndi kasupe wace adzauma, adzafunkha cuma ca akatundu onse ofunika.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 13