4. Anena mau akulumbira monama, pakucita mapangano momwemo; ciweruzo ciphuka ngati zitsamba zowawa m'micera ya munda.
5. Okhala m'Samariya adzaopera cifanizo ca ana a ng'ombe a ku Betaveni; pakuti anthu ace adzamva naco cisoni, ndi ansembe ace amene anakondwera naco, cifukwa ca ulemerero wace, popeza unacicokera.
6. Adzacitengeranso ku Asuri cikhale mphatso ya kwa mfumu Yarebu; Efraimu adzatenga manyazi, ndi Israyeli adzacita manyazi ndi uphungu wace.
7. Ndipo Samariya, mfumu yace yamwelera ngati thobvu pamadzi.
8. Ndipo misanje ya Aveni, ndiyo cimo la Israyeli, idzaonongeka; minga ndi mitungwi idzamera pa maguwa ao a nsembe; ndipo adzati kwa mapiri, Tiphimbeni; ndi kwa zitunda, Tigwereni.
9. Israyeli, wacimwa kuyambira masiku a Gibeya; pomwepo anaimabe; nkhondo ya pa ana a cosalungama siinawapeza ku Gibeya.
10. Pamene ndifuna ndidzawalanga, ndi mitundu ya anthu idzawasonkhanira pomangidwa iwo pa zolakwa zao ziwiri.
11. Ndipo Efraimu ndiye ng'ombe yaikazi yaing'ono, yozereweredwa, yokonda kupuntha tirigu; koma ndapita pa khosi lace lokoma; ndidzamsenzetsa Efraimu goli; Yuda adzalima, Yakobo adzaphwanya cibuluma cace.
12. Mudzibzalire m'cilungamo mukolole monga mwa cifundo; limani masala anu, pakuti yafika nthawi ya kufuna Yehova, mpaka afika Iye, nabvumbitsira inu cilungamo.
13. Mwalima coipa, mwakolola cosalungama, mwadya zipatso za mabodza; pakati watama njira yako ndi kucuruka kwa anthu ako amphamvu.