Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 1:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo anaimanso, nabala mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa iye, Umuche dzina lace Wosacitidwacifundo; pakuti sindidzacitiranso cifundo nyumba ya Israyeli, kuti ndiwakhululukire konse.

7. Koma ndidzacitira cifundo nyumba ya Yuda, ndi kuwapulumutsa mwa Ine Yehova Mulungu wao, osawapulumutsa ndi uta, kapena lupanga, kapena nkhondo ndi akavalo, kapena apakavalo.

8. Ataleka tsono kuyamwitsa Wosacitidwa cifundo, anaima, nabala mwana wamwamuna.

9. Ndipo Yehova anati, Umuche dzina lace Si-anthuanga; pakuti inu sindinu anthu anga, ndipo Ine sindine wanu.

10. Angakhale anatero, kuwerenga kwace kwa ana a Israyeli kudzanga mcenga wa kunyanja, wosayeseka kapena kuwerengeka; ndipo kudzatero kuti m'mene adawanena, Simuli anthu anga, adzanena nao, Muli ana a Mulungu wamoyo.

11. Ndipo ana a Yuda ndi ana a Israyeli adzasonkhanidwa pamodzi, nadzadziikira mkuru mmodzi, nadzakwera kucoka m'dziko; pakuti tsiku la Yezreeli ndi lalikuru.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 1