3. Mulungu anafuma ku Temani,Ndi Woyerayo ku phiri la Parana.Ulemerero wace unaphimba miyamba,Ndi dziko lapansi linadzala ndi kumlemekeza.
4. Ndi kunyezimira kwace kunanga kuunika;Anali nayo mitsitsi ya dzuwa yoturuka m'dzanja lace.Ndi komweko kunabisika mphamvu yace.
5. Patsogolo pace panapita mliri,Ndi makara amoto anaturuka pa mapaziace.
6. Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi;Anapenya, nanjenjemeretsa amitundu;Ndi mapiri acikhalire anamwazika,Zitunda za kale lomwe zinawerama;Mayendedwe ace ndiwo a kale lomwe.
7. Ndinaona mahema a Kusani ali mkusauka;Nsaru zocinga za dziko la Midyani zinanjenjemera.
8. Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje?Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi,Kapena ukali wanu panyanja,Kuti munayenda pa akavalo anu,Pa magareta anu a cipulumutso?
9. Munapombosola uta wanu;Malumbiro analumbirira mafuko anali mau oona.Munang'amba dziko lapansi ndi mitsinje.
10. Mapiri anakuonani, namva zawawa;Cigumula ca madzi cinapita;Madzi akuya anamveketsa mau ace,Nakweza manja ace m'mwamba.
11. Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao;Pa kuunika kwa mibvi yanu popita iyo.Pa kung'anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.
12. Munaponda dziko ndi kulunda,Munapuntha amitundu ndi mkwiyo.
13. Munaturukira cipulumutso ca anthu anu,Cipulumutso ca odzozedwa anu;Munakantha mutu wa nyumba yawoipa,Ndi kufukula maziko kufikira m'khosi.