Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 3:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndinamva, ndi m'mimba mwanga munabwadamuka,Milomo yanga inanthunthumira pamau,M'mafupa mwanga mudalowa cibvundi, ndipo ndinanjenjemera m'malo mwanga;Kuti ndipumule tsiku lamsauko,Pamene akwerera anthu kuti ayambane nao ndi makamu.

17. Cinkana mkuyu suphuka,Kungakhale kulibe zipatso kumpesa;Yalephera nchito ya azitona,Ndi m'minda m'mosapatsa cakudya;Ndi zoweta zacotsedwa kukhola,Palibenso ng'ombe m'makola mwao;

18. Koma ndidzakondwera mwa Yehova,Ndidzasekerera mwa Mulungu wa cipulumutso canga.

19. Yehova, Ambuye, ndiye mphamvuyanga,Asanduliza mapazi anga ngati a mbawala,Nadzandipondetsa pa misanje yanga.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 3