Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 3:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pemphero la Habakuku mneneri, pa Sigionoto.

2. Yehova, ndinamva mbiri yanu ndi mantha;Yehova, tsitsimutsani nchito yanu pakati pa zaka,Pakati pa zaka mudziwitse;Pa mkwiyo mukumbukile cifundo.

3. Mulungu anafuma ku Temani,Ndi Woyerayo ku phiri la Parana.Ulemerero wace unaphimba miyamba,Ndi dziko lapansi linadzala ndi kumlemekeza.

4. Ndi kunyezimira kwace kunanga kuunika;Anali nayo mitsitsi ya dzuwa yoturuka m'dzanja lace.Ndi komweko kunabisika mphamvu yace.

5. Patsogolo pace panapita mliri,Ndi makara amoto anaturuka pa mapaziace.

6. Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi;Anapenya, nanjenjemeretsa amitundu;Ndi mapiri acikhalire anamwazika,Zitunda za kale lomwe zinawerama;Mayendedwe ace ndiwo a kale lomwe.

7. Ndinaona mahema a Kusani ali mkusauka;Nsaru zocinga za dziko la Midyani zinanjenjemera.

8. Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje?Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi,Kapena ukali wanu panyanja,Kuti munayenda pa akavalo anu,Pa magareta anu a cipulumutso?

9. Munapombosola uta wanu;Malumbiro analumbirira mafuko anali mau oona.Munang'amba dziko lapansi ndi mitsinje.

10. Mapiri anakuonani, namva zawawa;Cigumula ca madzi cinapita;Madzi akuya anamveketsa mau ace,Nakweza manja ace m'mwamba.

11. Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao;Pa kuunika kwa mibvi yanu popita iyo.Pa kung'anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.

12. Munaponda dziko ndi kulunda,Munapuntha amitundu ndi mkwiyo.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 3