Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 2:2-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Yehova anandiyankha nati, Lembera masomphenyawo, nuwacenutse pamagome, kuti awawerenge mofulumira.

3. Pakuti masomphenyawo alindira nyengo yoikidwiratu, ndipo afulumirira potsirizira pace, osanama; akacedwa uwalindirire; popeza afika ndithu, osazengereza.

4. Taonani, moyo wace udzikuza, wosaongoka m'kati mwace; koma wolungama adzakhala ndi moyo mwa cikhulupiriro cace.

5. Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa cikhumbo cace ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsira amitundu onse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.

6. Kodi sadzamnenera fanizo onsewo, ndi mwambi womnyodola, ndi kuti, Tsoka iye wocurukitsa zimene siziri zace! mpaka liti? iye wodzisenzera zigwiriro.

7. Sadzauka kodi modzidzimuka iwo amene adzakuluma, ndi kugalamuka iwo amene adzakugwedezetsa; ndipo udzakhala zofunkha zao?

8. Popeza iwe wafunkha amitundu ambiri, otsala onse a mitundu ya anthu adzakufunkha iwe; cifukwa ca mwazi wa anthu, ndi ciwawa cocitikira dziko, mudzi, ndi onse okhalamo.

9. Tsoka iye wakupindulitsira nyumba yace phindu loipa, kuti aike cisanja cace ponyamuka, kuti alanditsidwe m'dzanja la coipa!

10. Wapangira nyumba yako camanyazi, pakuononga mitundu yambiri ya anthu, ndipo wacimwira moyo wako.

11. Pakuti mwala wa m'khoma upfuula, ndi mtanda wa kuphaso udzaubvomereza.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 2