Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 8:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. ndipo njiwa inadza kwa iye madzulo; ndipo, taonani, m'kamwa mwace munali tsamba lazitona lotyoledwa: ndipo anadziwa Nowa kuti madzi analimkuphwa pa dziko lapansi.

12. Ndipo analindanso masiku ena asanu ndi awiri; naturutsa njiwayo: ndipo siinabweranso konse kwa iye.

13. Ndipo panali caka ca mazana asanu ndi limodzi kudza cimodzi, mwezi woyamba, tsiku loyamba mwezi, madzi anaphwa pa dziko lapansi; ndipo Nowa anacotsa cindwi lace pacingalawa, nayang'ana, ndipo taonani, padauma pa dziko lapansi.

14. Mwezi waciwiri tsiku la makumi awiri kudza asanu ndi awiri la mwezi, lidauma dziko lapansi.

15. Mulungu ndipo ananena kwa Nowa, kuti,

16. Turukamoni m'cingalawamo, iwe ndi ana ako, ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.

17. Turutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse ziti ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi; kuti ziswane pa dziko lapansi, zibalane, zicuruke pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 8