Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 6:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndine, taonani, ndipo Ine ndidzadzetsa cigumula ca madzi pa dziko lapansi, kuti cionooge zamoyo zonse, m'mene muli mpweya wa moyo pansi pa thambo; zinthu zonse za m'dziko lapansi zidzafa.

18. Koma ndidzakhazikitsa ndi iwe pangano langa; ndipo udzalowa m'cingalawamo iwe ndi ana ako ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.

19. Ndipo zonse zokhala ndi moyo, ziwiri ziwiri za mtundu wao ulowetse m'cingalawamo, kuti zikhale ndi moyo pamodzi ndi iwe; zikhale zamphongo ndi zazikazi.

20. Za mbalame monga mwa mitundu yao, ndi zinyama monga mwa mitundu yao, ndi zokwawa zonse za dziko lapansi monga mwa mitundu yao, ziwiri ziwiri monga mwa mitundu yao, zidzadza kwa iwe kuti zikhale ndi moyo.

21. Ndipo iwe udzitengereko wekha zakudya zonse zodyedwa, oudzisonkhanitsire izi wekha: ndipo zidzakhala zakudya za iwe ndi za iwo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 6