Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 37:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo anatenga malaya ace a Yosefe, napha tonde, nabvika malaya m'mwazi wace:

32. natumiza malaya amwinjiro, nadza nao kwa atate ao: ndipo anati, Siwa tawatola; muzindikire tsono ngati ndi malaya a mwana wanu, kapena ndi ena.

33. Ndipo anazindikira nati, Ndiwo malaya a mwana wanga: wajiwa ndi cirombo: Yosefe wakadzulidwa ndithu.

34. Yakobo ndipo anang'amba malaya ace, nabvala ciguduli m'cuuno mwace namlirira mwana wace masiku ambiri.

Werengani mutu wathunthu Genesis 37