Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 37:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Israyeli anati kwa Yosefe, Kodi abale ako sadyetsa zoweta m'Sekemu? tiyeni, ndikutuma iwe kwa iwo. Ndipo anati, Ndine pano.

14. Ndipo anati kwa iye, Pita tsopano, nukaone ngati abale ako ali bwino, ndi ngati zoweta ziri bwino; nundibwezere ine mau. Ndipo anamtuma iye kucokera m'cigwa ca Hebroni, ndipo anadza ku Sekemu.

15. Ndipo anampeza munthu, taonani, analinkusokera m'thengo; munthuyo ndipo anamfunsa, nati, Kodi ufuna ciani?

16. Ndipo iye anati, Ndifuna abale anga. Undiuzetu kumene adyetsa zoweta.

17. Munthuyo ndipo anati, Anacoka pano; pakuti ndinamva alinkuti, Timuke ku Dotana. Yosefe ndipo anatsata abale ace, nawapeza ali ku Dotana.

Werengani mutu wathunthu Genesis 37