Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 32:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ngamila zamkaka makumi atatu ndi ana ao, ng'ombe zazikazi makumi anai, zazimuna khumi, aburu akazi makumi awiri ndi ana khumi.

16. Ndipo anazipereka zimenezo m'manja a anyamata ace, gulu pa lokha gulu pa lokha: ndipo anati kwa anyamata ace, Taolokani patsogolo panga, tacitani danga pakati pa magulu, tina ndi lina.

17. Ndipo anauza wotsogolera kuti, Pamene akomana nawe mkuru wanga Esau ndi kufunsa iwe kuti, Ndiwe yani, umuka kuti? za yani zimenezi patsogolo pako?

18. pomwepo uziti, Za kapolo wanu Yakobo; ndizo mphatso yotumizidwa kwa mbuyanga Esau; taonani ali pambuyo pathu.

19. Ndipo anauzanso waciwiri ndi wacitatu, ndi onse anatsata magulu, kuti, Muzinena kwa Esau cotero, pamene mukomana naye:

20. ndiponso muziti, Ndiponso, taonani, kapolo wanu Yakobo ali pambuyo pathu, Pakuti anati, Ndidzampembedzera iye ndi mphatso imene ipita patsogolo panga, pambuyo pace ndidzaona nkhope yace; kapena adzandilandira ine.

21. Momwemo naolotsa mphatso patsogolo pace: ndipo iye yekha anagona usiku womwewo pacigono.

22. Ndipo anauka usiku womwewo, natenga akazi ace awiri, ndi adzakazi ace awiri, ndi ana ace amuna khumi ndi mmodzi, naoloka pa doko la Yaboki.

23. Ndipo anawatenga iwo nawaolotsa pamtsinje, naziolotsa zonseanalinazo.

24. Ndipo anatsala Yakobo yekha; ndipo analimbana naye munthu kufikira mbandakuca.

25. Ndipo pamene anaona kuti sanamlaka, anakhudza nsukunyu ya ncafu yace; ndipo nsukunyu ya ncafu yace ya Yakobo inaguluka, pakulimbana naye.

26. Ndipo iye anati Ndileke ndimuke, cifukwa kulinkuca. Ndipo Yakobo anati, Sindidzakuleka iwe kuti umuke, ukapanda kundidalitsa ine.

27. Ndipo iye anati kwa Yakobo, Dzina lako ndani? Nati iye, Yakobo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 32