Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 31:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Yakobo anaona nkhope ya Labani, taonani, siinamuonekera iye monga kale.

3. Ndipo Yehova anati kwa Yakobo, Bwera ku dziko la atate wako, ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakhala ndi iwe.

4. Ndipo Yakobo anatumiza naitana Rakele ndi Leya adze kubusa ku zoweta zace,

5. ndipo anati kwa iwo, Ndiona ine nkhope ya atate wanu kuti siindionekera ine monga kale; koma Mulungu wa atate wanga anali ndi ine.

6. Ndipo inu mudziwa kuti ndi mphamvu zanga zonse ndatumikira atate wanu.

7. Ndipo atate wanu wandinyenga ine, nasinthanitsa malipilo anga kakhumi; koma Mulungu sanamlole iye andicitire ine coipa.

8. Akati cotero, Zamathotho-mathotho zidzakhala malipilo ako, zoweta zonse zinabala zamathotho-mathotho; ndipo akati iye cotere, Zamipyololo-mipyololo zidzakhala malipilo ako, ziweto zonse zinabala mipyololo-mipyololo.

9. Comweco Mulungu anazicotsa zoweta za atate wanu, nandipatsa ine.

Werengani mutu wathunthu Genesis 31