Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 30:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Yakobo anapsa mtima ndi Rakele; nati, Kodi ine ndikhala m'malo a Mulungu amene akukaniza iwe zipatso za mimba?

3. Ndipo Rakele anati, Taonani mdzakazi wanga Biliha, mulowe kwa iye; ndipo iye adzabala pa maondo anga, kuti inenso ndionerepo ana pa iye.

4. Ndipo Rakele anampatsa iye Biliha mdzakazi wace akhale mkazi wace; ndipo Yakobo analowa kwa iye.

5. Ndipo Biliha anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna.

Werengani mutu wathunthu Genesis 30