Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 3:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo anati Yehova Mulungu kwa njokayo, Cifukwa kuti wacita ici, wotembereredwa ndiwe wopambana ndi zinyama zonse ndi zamoyo zonse za m'thengo: uziyenda ndi pamimba pako, uzidya pfumbi masiku onse a moyo wako:

15. ndipo ndidzaika udani pakati pa iwe ndi mkaziyo, ndi pakati pa mbeu yako ndi mbeu yace; ndipo idzalalira mutu wako, ndipo iwe udzalalira citende cace.

16. Kwa mkaziyo ndipo anati, Ndidzacurukitsa kusauka kwako ndi potenga mimba pako; udzasauka pakubala: udzakhumba mwamuna wako, ndipo iye adzakulamulira iwe.

17. Kwa Adamu ndipo anati, Cifukwa kuti wamvera mau a mkazi wako, nudya za mtengo umene ndinakuuza iwe kuti, Usadyeko; nthaka ikhale yotembereredwa cifukwa ca iwe; m'kusauka udzadyako masiku onse a moyo wako:

18. minga ndi mitula idzakubalira iwe; ndipo udzadya therere la m'thengo:

19. m'thukuta la nkhope yako udzadya cakudya, kufikira kuti udzabwerera kunthaka: cifukwa kuti m'menemo unatengedwa: cifukwa kuti ndiwe pfumbi, ndi kupfumbiko udzabwerera.

20. Ndipo mwamuna anamucha dzina la mkazi wace, Hava; cifukwa ndiye amace wa amoyo onse.

21. Yehova Mulungu ndipo anapangira Adamu ndi mkazi wace maraya azikopa, nawabveka iwo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 3