Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 29:24-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo Labani anampatsa mwana wace wamkazi Leya Zilipa mdzakazi wace kuti akhale mdzakazi wa Leya.

25. Ndipo panali m'mamawa, anaona kuti ndi Leya; ndipo anati kwa Labani, Ciani wandicitira ine? Kodi sindinakutumikira iwe cifukwa ca Rakele? wandinyenga ine bwanji?

26. Ndipo Labani anati, Satero kwathu kuno, kupatsa wamng'ono asanapatse wamkuru.

27. Umarize sabata lace la uyu, ndipo ndidzakupatsa uyonso cifukwa ca utumiki umene udzanditumikirawo kuonjezera zaka zina zisanu ndi ziwiri.

28. Yakobo ndipo anacita cotero namariza sabata lace; ndipo Labani anampatsa iye Rakele mwana wace wamkazi kuti akwatire iyenso.

29. Ndipo Labani anampatsa mwana wace wamkazi Rakele Biliha mdzakazi wace kuti akhale mdzakazi wa Rakele.

30. Ndipo Yakobo analowanso kwa Rakele, namkondanso Rakele kopambana Leya, namtumikira Labani zaka zisanu ndi ziwiri zinanso.

31. Pamene Yehova anaona kuti anamuda Leva, anatsegula m'mimba mwace; koma Rakele anali wouma.

Werengani mutu wathunthu Genesis 29