Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 28:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndiponso kuti pamene anamdalitsa iye, anamuuza iye kuti, Usatenge mkazi wa ana akazi a Kanani; ndiponso kuti Yakobo anamvera atate wace ndi amace, nanka ku Padanaramu;

8. ndipo Esau anaona kuti ana akazi a Kanani sanakondweretsa Isake atate wace:

9. ndipo ananka kwa Ismayeli, naonjezera kwa akazi amene anali nao, natenga Mahalati mwana wamkazi wa Ismayeli mwana wa Abrahamu, mlongo wace wa Nebayoti akhalemkazi wace.

10. Ndipo Yakobo anacoka m'Beereseba, nanka ku Harana.

11. Ndipo anafika kumalo, nagona kumeneko usiku, cifukwa lidalowa dzuwa: ndipo anatenga mwala wa kumeneko, nauika pansi pa mutu wace, nagona tulo kumeneko.

Werengani mutu wathunthu Genesis 28