Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 27:43-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Ndipo tsopane mwana wanga, tamvera mau anga: tauka, nuthawire kwa Labani mlongo wanga ku Harana;

44. ukhale naye masiku akuwerengeka, mpaka wamcokera ukali wa mkuru wako;

45. mpaka wakucokera mkwiyo wa mkuru wako, kuti aiwale cimene wamcitira iye; pamenepo ndipo ndidzatumiza kukutenganso iwe kumeneko; ndidzakhala bwanji wopanda inu nonse awiri tsiku limodzi?

46. Ndipo anati Rebeka kwa Isake, Ndalema moyo wanga cifukwa ca aria akazi a Heti: akatenga Yakobo mkazi wa ana akazi a Heti, onga ana akazi a m'dziko lino, moyo wanga udzandikhalira ine bwanji?

Werengani mutu wathunthu Genesis 27