Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 27:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo Isake atate wace anati kwa iye, Senderatu, undimpsompsone mwana wanga.

27. Ndipo anasendera nampsompsona; ndipo anamva kununkhira kwa zobvala zace, namdalitsa, nati,Taona, kununkhira kwa mwana wanga,Kufanana ndi kununkhira kwa munda anaudalitsa Yehova;

28. Mlungu akupatse iwe mame a kumwamba,Ndi zonenepa za dziko lapansi,Ndi tirigu wambiri ndi vinyo;

29. Anthu akutumikire iwe,Mitundu ikuweramire iwe;Ucite ufumu pa abale ako,Ana a amako akuweramire iwe;Wotemberereka ali yense akutemberera iwe,Wodalitsika ali yense akudalitsa iwe.

30. Ndipo panali atatha Isake kumdalitsa Yakobo, ataturuka Yakobo pamaso pa Isake atate wace, Esau mkuru wace analowa kucokera kuthengo,

31. Ndipo iyenso anakonza cakudya cokolera, nadza naco kwa atate wace, nati kwa atate wace, Auke atate wanga, adye nyama ya mwana wace, kuti moyo wanu undidalitse ine.

Werengani mutu wathunthu Genesis 27