Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 26:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anyamata a Isake anakumba m'cigwa, napeza kumeneko citsime ca madzi otumphuka.

20. Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isake kuti, Madzi ndi athu; ndipo anacha dzina la citsimeco Eseke: cifukwa anakangana nave.

21. Ndipo anakumbanso citsime cina, ndipo anakangana naconso; nacha dzina lace Sitina.

22. Ndipo anacoka kumeneko nakumba citsime cina; koma sanakangana naco cimeneco; ndipo anacha dzina lace Rehoboti; ndipo anati, Cifukwa kuti tsopano Yehova anatipatsa ife malo, ndipo tidzabalana m'dziko muno.

23. Ndipo anacoka kumeneko nakwera kunka ku Beereseba,

24. Ndipo Yehova anamuonekera iye usiku womwewo, nati, Ine dine Mulungu wa Abrahamu atate wako; usaope, cifukwa kuti Ine ndiri ndi iwe, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kucurukitsa mbeu zako, cifukwa ca Abrahamu kapolo wanga.

Werengani mutu wathunthu Genesis 26