Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 26:11-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Abimeleke anauza anthu ace, nati, Ali yense amene akhudza mwamuna uyo kapena mkazi wace, zoonatu adzaphedwa.

12. Ndipo Isake anabzala m'dzikomo, nalandira za makumi khumi caka cimeneco; ndipo Yehova anamdalitsa iye.

13. Ndipo anakula munthuyo, nakulakula kufikira kuti anakhala wamkurukuru:

14. ndipo anali ndi cuma ca nkhosa, ndi cuma ca zoweta, ndi banja lalikuru: ndipo Afilisti anamcitira iye nsanje.

15. Ndipo zitsime zonse anakumba anyamata a atate wace Afilisti anazitseka, nazikwirira ndi dothi.

16. Ndipo Abimeleke anati kwa Isake, Ucoke kwa ife cifukwa kuti iwe uti wamkuru wopambana ife.

17. Ndipo Isake anacoka kumeneko, namanga hema wace m'cigwa ca Gerari, nakhala kumeneko.

18. Ndipo Isake anafukulanso zitsime za madzi, anazikumba masiku a Abrahamu atate wace; cifukwa kuti Afilisti anazitseka atafa Abrahamu: ndipo anazicha maina monga maina omwe anazicha atate wace.

19. Ndipo anyamata a Isake anakumba m'cigwa, napeza kumeneko citsime ca madzi otumphuka.

20. Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isake kuti, Madzi ndi athu; ndipo anacha dzina la citsimeco Eseke: cifukwa anakangana nave.

21. Ndipo anakumbanso citsime cina, ndipo anakangana naconso; nacha dzina lace Sitina.

22. Ndipo anacoka kumeneko nakumba citsime cina; koma sanakangana naco cimeneco; ndipo anacha dzina lace Rehoboti; ndipo anati, Cifukwa kuti tsopano Yehova anatipatsa ife malo, ndipo tidzabalana m'dziko muno.

23. Ndipo anacoka kumeneko nakwera kunka ku Beereseba,

24. Ndipo Yehova anamuonekera iye usiku womwewo, nati, Ine dine Mulungu wa Abrahamu atate wako; usaope, cifukwa kuti Ine ndiri ndi iwe, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kucurukitsa mbeu zako, cifukwa ca Abrahamu kapolo wanga.

25. Ndipo anamanga kumeneko guwa la nsembe, naitana dzina la Yehova, namanga hema wace kumeneko: ndi pamenepo anyamata a Isake anakumba citsime.

26. Ndipo ananka kwa iye Abimeleke kucokera ku Gerari, ndi Ahuzati bwenzi lace, ndi Fikoli, kazembe wa nkhondo yace.

27. Ndipo Isake anati kwa iwo, Mwandidzera cifukwa ciani, inu akundida ine, ndi kundicotsa kwanu?

28. Ndipo iwo anati, Kuona tinaona kuti Yehova ali ndi iwe; ndipo tinati, Tilumbiriranetu tonse awiri, ife ndi iwe, ticite pangano ndi iwe;

Werengani mutu wathunthu Genesis 26