Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 25:25-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo woyamba anabadwa wofiira, monse mwace monga maraya aubweya; ndipo anamucha dzina lace Esau.

26. Pambuyo pace ndipo anabadwa mphwace ndipo dzanja lace linagwira citende ca Esau, ndi dzina lace linachedwa Yakobo: ndipo Isake anali wa zaka makumi asanu ndi limodzi pamene mkazi wace anabala iwo.

27. Ndipo anakula anyamatawo; ndipo Esau anali munthu wakudziwa zakusaka nyama, munthu wa m'thengo; ndipo Yakobo anali munthu wofatsa, wakukhala m'mahema.

28. Ndipo Isake anakonda Esau, cifukwa anadya nyama yace ya m'thengo; koma Rebeka anakonda Yakobo,

29. Ndipo Yakobo anaphika mphodza: ndipo Esau anacokera kuthengo, nalefuka:

30. ndipo Esau anati kwa Yakobo, Undipatse ndidye cofiiraco; cifukwa ndalefuka: cifukwa cace anamucha dzina lace Edomu.

31. Ndipo Yakobo anati, Tigulane lero ukulu wako.

Werengani mutu wathunthu Genesis 25