Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 24:65-67 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

65. Ndipo anati kwa mnyamata, Munthuyo ndani amene ayenda m'munda kukomana ndi ife? Mnyamatayo ndipo anati, Uyo ndi mbuyanga: cifukwa cace namwali anatenga cophimba cace nadziphimba.

66. Mnyamatayo ndipo anamuuza Isake zonse anazicita.

67. Ndipo Isake anamlowetsa mkaziyo m'hema wa amace Sara, namtenga Rebeka, nakhala iye mkazi wace; ndipo anamkonda iye; ndipo Isake anatonthozedwa mtima atafa amace.

Werengani mutu wathunthu Genesis 24