Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 22:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo panali zitapita zimenezo, Mulungu anamuyesa Abrahamu nati kwa iye, Abrahamu; ndipo anati, Ndine pano.

2. Ndipo anati, Tengatu mwana wako, wamwamuna wayekhayo, Isake, amene ukondana naye, numuke ku dziko la Moriya; numpereke iye kumeneko nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri lomwe ndidzakuuza iwe.

3. Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa namanga buru wace, natengako anyamata ace awiri pamodzi naye, ndi Isake mwana wace, nawaza nkhuni za nsembe, nauka, nanka kumalo komwe Mulungu anamuuza iye,

4. Tsiku lacitatu Abrahamu anatukula maso ace naona malowo patari.

5. Ndipo Abrahamu anati kwa anyamata ace, Khalani kuno ndi buru, ine ndi mwanayu tinka uko, ndipo tikapemphera ndi kubweranso kwa inu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 22