Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 21:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa, natenga mkate ndi mcenje wa madzi, nampatsa Hagara, naika paphewa pace, ndi mwana, namcotsa iye: ndipo iye anamuka, nasocerera m'cipululu ca Beereseba.

15. Ndipo anatha madzi a m'mcenje ndipo anaika mwana pansi pa citsamba.

16. Ndipo ananka nakhala pansi popenyana naye patari, monga pakugwa mubvi: cifukwa anati, Ndisaone kufa kwa mwana. Ndipo anakhala popenyana naye, nakweza mau ace nalira,

17. Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? usaope; cifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.

18. Tauka, nuukitse mnyamatayo, ndi kumgwira m'dzanja lako; cifukwa ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.

19. Ndipo Mulungu anamtsegula m'maso mwace, ndipo anaona citsime ca madzi; namuka nadzaza mcenje ndi madzi, nampatsa mnyamata kuti amwe.

20. Ndipo Mulungu anakhala ndi mnyamata, ndipo anakula iye; nakhala m'cipululu, nakhala wauta.

21. Ndipo anakhala m'cipululu ca Parana; ndipo amace anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Aigupto.

Werengani mutu wathunthu Genesis 21