Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 19:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndipo anamuitana Loti, nati kwa iye, Ali kuti anthu amene anadza kwa iwe madzulo ano, utiturutsire iwo kuti tiwadziwe.

6. Ndipo Loti anaturukira kwa iwo pakhomo, natseka cambuyo pakhomo pace.

7. Ndipo anati, Abale anga, musacitetu koipa kotere.

8. Taonanitu, ndiri ndi ana akazi awiri, amene sanadziwe mwamuna; ndiwaturutsire iwo kwa inu, mucite nao comwe cikomera inu; koma anthu awa musawacitire iwo kanthu; cifukwa kuti anadza iwo pansi pa mthunzi wa cindwi langa,

9. Ndipo anati iwo, Baima; natinso, Uyu anadza kuno kukhala ngati mlendo, ndipo afuna kutilamulira; tsopano tidzakucitira iwe koipa koposa iwo. Ndipo iwo anamkakamiza munthuyo Loti ndithu, nayandikira kuti aswe citseko.

10. Komo anthu aja anaturutsa dzanja lao, namlowetsa Loti momwe anali iwo m'nyumba, natseka pakhomo,

Werengani mutu wathunthu Genesis 19