Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 44:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo akaturukira ku bwalo lakunja, ku bwalo lakunja kuti anthu, azibvula zobvala zao zimene atumikira nazo, naziike m'zipinda zopatulika, nabvale zobvala zina; angapatule anthu ndi zovala zao.

20. Ndipo asamete mitu yao, kapena asalekerere nzera za tsitsi lao zikule, azingosenga mitu yao.

21. Kungakhale kumwa vinyo, wansembe asamwe polowa ku bwalo la m'katimo.

22. Kungakhale kutenga amasiye kapena osudzulidwa akhale akazi ao, asacite; koma atenge anamwali a mbeu ya nyumba ya Israyeli, kapena wamasiye ndiye wamasiye wa wansembe.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 44