Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 38:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. motero kuti nsomba za m'nyanja, ndi mbalame za m'mlengalenga, ndi nyama za kuthengo, ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, ndi anthu onse akukhala padziko, zidzanjenjemera pamaso panga; ndi mapiri adzagwetsedwa, ndi potsetsereka padzagumuka, ndi makoma onse adzagwa pansi.

21. Ndipo ndidzamuitanira lupanga ku mapiri anga onse, ati Ambuye Yehova, munthu ali yense lupanga lace lidzaombana nalo la mbale wace.

22. Ndipo ndidzalimbana naye ndi mliri ndi mwazi; ndipo ndidzambvumbitsira iye, ndi magulu ace, ndi mitundu yambiri ya anthu okhala naye mbvumbi waukuru, ndi matalala akuru, moto ndi sulfure.

23. Momwemo ndidzadzikuzitsa, ndi kudzizindikiritsa woyera, ndipo ndidzadziwika pamaso pa amitundu ambiri; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 38