26. Ndipo ndidzapangana nao pangano la mtendere, lidzakhala pangano losatha nao, ndipo ndidzawakhazika, ndi kuwacurukitsa, ndi kuika malo anga opatulika pakati pao kosatha.
27. Kacisi wanganso adzakhala nao, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wao, ndi iwo adzakhala anthu anga.
28. Ndipo amitundu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova wakupatula Israyeli, pokhala pakati pao malo anga opatulika kosatha.