Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 33:16-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Zoipa zace ziri zonse anazicita sizidzakumbukika zimtsutse, anacita coyenera ndi colungama; adzakhala ndi moyo ndithu.

17. Koma ana a anthu a mtundu wako akuti, Njira ya Ambuye siiyenera; koma iwowa njira yao siiyenera.

18. Akabwerera wolungama kuleka cilungamo cace, nakacita cosalungama, adzafa m'mwemo.

19. Ndipo woipa akabwerera kuleka coipa cace, nakacita coyenera ndi colungama, adzakhala ndi moyo nazo.

20. Koma munati, Njira ya Ambuye siiyenera. Nyumba ya Israyeli inu, ndidzakuweruzani, yense monga mwa njira zace.

21. Ndipo kunali caka cakhumi ndi ciwiri ca undende wathu, mwezi wakhumi, tsiku lacisanu la mweziwo, anandidzera wina wopulumuka ku Yerusalemu, ndi kuti, Wakanthidwa mudzi.

22. Koma dzanja la Yehova linandikhalira madzulo, asanandifike wopulumukayo; ndipo ananditsegula pakamwa mpaka anandifika m'mawa, m'mwemo panatseguka pakamwa panga, wosakhalanso wosalankhula.

23. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

24. Wobadwa ndi munthu iwe, iwo okhala ku mabwinja a dziko la Israyeli anena, ndi kuti, Abrahamu anali yekha, nakhala nalo dziko colowa cace; koma ife ndife ambiri, dzikoli lipatsidwa kwa ife colowa cathu.

25. Cifukwa cace unene nao, Atero Ambuye Yehova, Mumadyera kumodzi ndi mwazi, mumakwezera maso anu ku mafano anu, ndi kukhetsa mwazi; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko colowa canu?

26. Mumatama lupanga lanu, mumacita conyansa, mumaipsa yense mkazi wa mnansi wace; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko colowa canu?

27. Uzitero nao, Atero Ambuye Yehova, Pali Ine, iwo okhala kumabwinja adzagwadi ndi lupanga, ndi iye ali kuthengo koyera ndidzampereka kwa zirombo, adyedwe nazo; ndi iwo okhala m'malinga ndi m'mapanga adzafa ndi mliri.

28. Ndipo ndidzasanduliza dziko likhale lacipululu ndi lodabwitsa, ndi mphamvu yace yodzikuza idzatha, ndi mapiri a Israyeli adzakhala acipululu, osapitako munthu.

29. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, posanduliza Ine dziko likhale lacipululu ndi lodabwitsa, cifukwa ca zonyansa zao zonse anazicita.

30. Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, ana a anthu a mtundu wako anena za iwe ku makoma ndi ku makomo a nyumba zao, nanenana yense ndi mbale wace, ndi kuti, Tiyeni tikamve mau ofuma kwa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 33