Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 32:13-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndidzaononganso nyama zace zonse za ku madzi ambiri; ndi phazi la munthu silidzabvundulira, ndi ziboda za nyama zosawabvundulira.

14. Pamenepo ndidzadikhitsa madzi ace, ndi kuyendetsa madzi a m'mitsinje mwao ngati mafuta, ati Ambuye Yehova.

15. Pakusanduliza Ine dziko la Aigupto likhale lopasuka ndi labwinja, dziko losowa zodzaza zace, pakukantha Ine onse okhala m'mwemo, pamenepo adzadziwa kuti ine ndine Yehova.

16. Iyi ndi nyimbo ya maliro adzalira nayo, ana akazi a amitundu adzacita nayo maliro; adzalirira nayo Aigupto ndi aunyinji ace onse, ati Ambuye Yehova.

17. Kunalinso caka cakhumi ndi ciwiri, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi, anandidzera mau a Yehova, ndi kuti,

18. Wobadwa ndi munthu iwe, lirira aunyinji a Aigupto, nuwagwetsere iye ndi ana akazi a amitundu omveka kunsi kwa dziko, pamodzi ndi iwo akutsikira kudzenje.

19. Uposa yani m'kukoma kwako? tsika, nuikidwe ndi osadulidwa.

20. Adzagwa pakati pa iwo ophedwa ndi lupanga, operekedwa kwa lupanga, mkokereko ndi aunyinji ace onse.

21. Amphamvu oposa ali m'kati mwa manda adzanena naye, pamodzi ndi othandiza ace, Anatsikira, agonako osadulidwawo, ophedwa ndi lupanga,

22. Asuri ali komwe ndi msonkhano wace wonse, manda ace amzinga; ophedwa onsewo, adagwa ndi lupanga;

23. manda ao aikidwa ku malekezero a dzenje, ndi gulu lace lizinga manda ace; ophedwa onsewo adagwa ndi lupanga, amene anaopsetsa m'dziko la amoyo.

24. Elamu ali komwe ndi gulu lace lonse lozinga manda ace; ophedwa onsewo, adagwa ndi lupanga; amene anatsikira osadulidwa kunsi kwace kwa dziko, amene anaopsetsa m'dziko la amoyo, nasenza manyazi ao, pamodzi ndi iwo akutsikira kudzenje.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 32