Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 3:9-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndalimbitsa mutu wako woposa mwala wolimbitsitsa, usawaopa kapena kutenga nkhawa pamaso pao; pakuti iwo ndiwo nyumba yopanduka.

10. Ananenanso nane, Wobadwa ndi munthu iwe, mau anga onse ndidzawanena ndi iwe uwalandire m'mtima mwako, utawamva m'makutu mwako.

11. Numuke, nufike kwa andende kwa ana a anthu a mtundu wako, nunene nao ndi kuwauza, Atero Yehova Mulungu, ngakhale akamva kapena akaleka kumva.

12. Pamenepo mzimu unandinyamula, ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mau a mkokomo waukuru, ndi kuti, Wodala ulemerero wa Yehova m'malo mwace.

13. Ndipo ndinamva mkokomo wa mapiko a zamoyozo pakukhudzana, ndi mlikiti wa njingazo m'mbali mwa izo, ndilo phokoso la mkokomo waukuru.

14. M'mwemo mzimu unandinyamula ndi kucoka nane; ndipo ndinamuka wowawidwa, womyuka mtima; koma dzanja la Yehova linandigwirizitsa,

15. Ndipo ndinafika kwa andende ku Telabibu, okhala kumtsinje Kebara, ndiko kwao; ndipo ndinakhalako woda bwa pakati pao masiku asanu ndi awiri.

16. Ndipo kunali atatha masiku asanu ndi awiri, mau a Yehova anandidzera, ndi kuti,

17. Wobadwa ndi munthu iwe, ndakuika ukhale mlonda wa nyumba ya Israyeli, m'mwemo mvera mau oturuka m'kamwa mwanga, nundicenjezere iwo.

18. Ndikanena kwa woipa, Udzafa ndithu, koma iwe osamcenjeza, wosanena kumcenjeza woipayo aleke njira yace yoipa, kumsunga ndi moyo, woipa yemweyo adzafa mu mphulupulu yace; koma mwazi wace ndidzaufuna pa dzanja lako.

19. Koma ukacenjeza woipa, osabwerera iye kuleka coipa cace kapena njira yace yoipa, adzafa mu mphulupulu yace; koma iwe walanditsamoyo wako.

20. Momwemonso akabwerera wolungama kuleka cilungamo cace, ndi kucita cosalungama, ndipo ndikamuikira comkhumudwitsa, adzafa; popeza sunamcenjeza, adzafa m'cimo lace, ndi zolungama zace adazicita sizidzakumbukika; koma mwazi wace ndidzaufuna pa dzanja lako.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 3