Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 28:2-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Wobadwa ndi munthu iwe, uziti kwa kalonga wa Turo, Atero Ambuye Yehova, Popeza mtima wako wadzikweza, nuti, Ine ndine mulungu, ndikhala pa mpando wa Mulungu pakati pa nyanja, ungakhale uli munthu, wosati Mulungu, ungakhale waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu,

3. taona, ndiwe wanzeru woposa Danieli, palibe cinsinsi angakubisire;

4. mwa nzeru zako ndi luntha lako wadzionerera cuma, wadzionereranso golidi ndi siliva mwa cuma cako;

5. mwa nzeru zako zazikuru ndi kugulana malonda kwako wacurukitsa cuma cako, ndi mtima wako wadzikuza cifukwa ca cuma cako;

6. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu;

7. cifukwa cace taona, ndidzakufikitsira alendo oopsa a mitundu ya anthu, iwo adzasololera malupanga ao nzeru zako zokongola, nadzaipsa kunyezimira kwako.

8. Adzakutsitsira kumanda, nudzafa mafedwe a ophedwa m'kati mwa nyanja.

9. Kodi udzanena ndithu pamaso pa iye wakupha iwe, Ine ndine Mulungu, pokhala uli munthu, wosati Mulungu, m'dzanja la iye wakupha iwe.

10. Udzafa mafedwe a osadulidwa ndi dzanja la alendo, pakuti ndacinena, ati Ambuye Yehova.

11. Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,

12. Wobadwa ndi munthu iwe, kweza nyimbo ya maliro yolirira mfumu ya Turo, nuziti kwa iye, Atero Ambuye Yehova, Wakomera muyeso ndi cizindikilo, wodzala ndi nzeru wokongola wangwiro.

13. Unali m'Edene, munda wa Mulungu, mwala uli wonse wa mtengo wace unali copfunda cako, sardiyo, topazi, diamondi, berulo, sohamu, ndi yaspi, safiro, nofeki, bareketi, ndi golidi; malingaka ako ndi akazi ako anakutumikira tsiku lolengedwa iwe zinakonzekeratu.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 28