Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 27:9-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Akr-ru a ku Gebala ndi eni luso ace anali mwa iwe kukonza ziboo zako; zombo zonse za kunyanja pamodzi ndi amarinyero ao anali mwa iwe kusinthana nawe malonda.

10. Aperisiya, Aludi, Apuri, anali m'khamu lako; anthu ako a nkhondo anapacika cikopa ndi cisoti mwa iwe, anamveketsa kukoma kwako.

11. Anthu a Ativadi pamodzi ndi ankhondo ako anali pa malinga ako pozungulira, ndi Agamadi anali mu nsanja zako; anapacika zikopa zao pa makoma ako pozungulira, anakwaniritsa kukoma kwako.

12. Tarisi anagulana nawe malonda m'kucuruka kwa cuma ciri conse; anagula malonda ako ndi siliva ndi citsulo, seta ndi ntobvu.

13. Yavani, Tuba, Meseke, anagulana nawe malonda; ndi anthu amoyo ndi zotengera zamkuwa anagulana nawe malonda.

14. Iwo a nyumba ya Togarima anagula malonda ako ndi akavalo, ndi akavalo a nkhondo, ndi nyuru.

15. Anthu a ku Dedani anakutsatsa malonda, zisumbu zambiri zinazolowerana nawe malonda ako, anabwera nazo minyanga ndi phingo kugulana nawe malonda.

16. Aramu anacita nawe malonda cifukwa ca zambirizo udazipanga, anagula malonda ako ndi smaragido, nsaru yofiirira, ndi yopikapika, ndi bafuta, ndi korale, ndi ngale.

17. Yuda ndi dziko la Israyeli anagulana nawe malonda, anagula malonda ako ndi tirigu wa ku Miniti, ndi zozuna, ndi uci, ndi mafuta, ndi mafuta amankhwala.

18. Damasiko anagulana nawe malonda cifukwa ca zambirizo udazipanga, cifukwa ca kucuruka kwa cuma ciri conse, ndi vinyo wa ku Keliboni, ndi ubweya wa nkhosa woyera.

19. Vedani ndi Yavani anagula malonda ako ndi thonje, unagulana nao citsulo cosalala, ngaho, ndi mzimbe.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 27