Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 26:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Nadzaikira malinga ako zogumulira, nadzagwetsa nsanja zako ndi zida zace.

10. Papeza acuruka akavalo ace, pfumbi lao lidzakukuta; malinga ako adzagwedezeka ndi phokoso la apakavalo, ndi njinga za magareta, palowa iye pa zipata zako, monga umo amalowera m'mudzi popasukira linga lace.

11. Ndi ziboda za akavalo ace iye adzapondaponda m'makwalala ako onse; adzapha anthu ako ndi lupanga; ndi zoimiritsa za mphamvu yako zidzagwa pansi.

12. Ndipo adzalanda cuma cako ndi kufunkha malonda ako, nadzagwetsa malinga ako ndi kupasula nyumba zako zofunika, nadzaponya miyala yako, ndi mitengo yako, ndi pfumbi lako, m'madzi.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 26