Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 26:8-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ana ako akazi adzawapha kumunda ndi lupanga; ndipo adzakumangira nsanja, ndi kukuundira mtumbira, ndi kukuimikira cikopa.

9. Nadzaikira malinga ako zogumulira, nadzagwetsa nsanja zako ndi zida zace.

10. Papeza acuruka akavalo ace, pfumbi lao lidzakukuta; malinga ako adzagwedezeka ndi phokoso la apakavalo, ndi njinga za magareta, palowa iye pa zipata zako, monga umo amalowera m'mudzi popasukira linga lace.

11. Ndi ziboda za akavalo ace iye adzapondaponda m'makwalala ako onse; adzapha anthu ako ndi lupanga; ndi zoimiritsa za mphamvu yako zidzagwa pansi.

12. Ndipo adzalanda cuma cako ndi kufunkha malonda ako, nadzagwetsa malinga ako ndi kupasula nyumba zako zofunika, nadzaponya miyala yako, ndi mitengo yako, ndi pfumbi lako, m'madzi.

13. Ndipo ndidzaleketsa phokoso la nyimbo zako, ndi kulira kwa mazeze ako sikudzamvekanso.

14. Ndipo ndidzakuyesa pathanthwe poyera; udzakhala poyanika khoka, sadzakumanganso; pakuti Ine Yehova ndacinena, ati Ambuye Yehova.

15. Atero Ambuye Yehova kwa Turo, Zisumbu sizidzagwedezeka nanga pomveka kugwa kwako, pabuula olasidwa, pakucitika kuphako pakati pako?

16. Pamenepo akalonga onse a kunyanja adzatsika ku mipando yacifumu yao, nadzabvula zobvala zao zopikapika, nadzabvala kunjenjemera, nadzakhala panthaka pansi, nadzanjenjemera mphindi zonse ndi kukudabwa.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 26