Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 23:24-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo adzakudzera ndi zida, magareta a nkhondo, ndi magareta ena, pamodzi ndi msonkhano wa mitundu ya anthu; adzadziikira pozungulira pako ndi zikopa zocinjiriza ndi zisoti; ndipo ndidzawaika aweruze, nadzakuweruza monga mwa maweruzo ao.

25. Ndipo ndidzakuikira nsanje yanga, nadzakucitira mwaukali, iwowa adzakudula mphuno ndi makutu; ndi otsiriza ako adzagwa ndi lupanga, adzakucotsera ana ako amuna ndi akazi, ndi otsirizira ako adzatha ndi moto.

26. Adzakubvulanso zobvala zako, ndi kukucotsera zokometsera zako zokongola.

27. Motero ndidzakuleketsera coipa cako, ndi cigololo cako cocokera m'dziko la Aigupto; ndipo sudzazikwezeranso maso ako, kapena kukumbukiranso Aigupto,

28. Pakuti atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakupereka m'dzanja la iwo amene uwada, m'dzanja la iwo amene moyo wako ufukidwa nao;

29. ndipo adzacita nawe mwaudani, nadzalanda zonse udazigwirira nchito, nadzakusiya wamarisece ndi wausiwa; ndi umarisece wa zigololo zako udzabvulidwa, dama lako ndi zigololo zako zomwe.

30. Izi adzakucitira cifukwa watsata amitundu, ndi kucita nao cigololo, popezanso wadetsedwa ndi mafano ao.

31. Wayenda m'njira ya mkuru wako, cifukwa cace ndidzapereka cikho cace m'dzanja lako.

32. Atero Ambuye Yehova, M'cikho ca mkuru wako udzamweramo ndico cacikuru ngati mcenje; adzakuseka pwepwete, nadzakunyoza muli zambiri m'menemo.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 23