Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 23:23-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. a ku Babulo, ndi Akasidi, Pekodi, ndi Sowa, ndi Kowa, ndi Aasuri onse pamodzi nao, anyamata ofunika, ziwanga ndi akazembe onsewo, akalonga ndi mandoda onsewo, oyenda ndi akavalo.

24. Ndipo adzakudzera ndi zida, magareta a nkhondo, ndi magareta ena, pamodzi ndi msonkhano wa mitundu ya anthu; adzadziikira pozungulira pako ndi zikopa zocinjiriza ndi zisoti; ndipo ndidzawaika aweruze, nadzakuweruza monga mwa maweruzo ao.

25. Ndipo ndidzakuikira nsanje yanga, nadzakucitira mwaukali, iwowa adzakudula mphuno ndi makutu; ndi otsiriza ako adzagwa ndi lupanga, adzakucotsera ana ako amuna ndi akazi, ndi otsirizira ako adzatha ndi moto.

26. Adzakubvulanso zobvala zako, ndi kukucotsera zokometsera zako zokongola.

27. Motero ndidzakuleketsera coipa cako, ndi cigololo cako cocokera m'dziko la Aigupto; ndipo sudzazikwezeranso maso ako, kapena kukumbukiranso Aigupto,

28. Pakuti atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakupereka m'dzanja la iwo amene uwada, m'dzanja la iwo amene moyo wako ufukidwa nao;

29. ndipo adzacita nawe mwaudani, nadzalanda zonse udazigwirira nchito, nadzakusiya wamarisece ndi wausiwa; ndi umarisece wa zigololo zako udzabvulidwa, dama lako ndi zigololo zako zomwe.

30. Izi adzakucitira cifukwa watsata amitundu, ndi kucita nao cigololo, popezanso wadetsedwa ndi mafano ao.

31. Wayenda m'njira ya mkuru wako, cifukwa cace ndidzapereka cikho cace m'dzanja lako.

32. Atero Ambuye Yehova, M'cikho ca mkuru wako udzamweramo ndico cacikuru ngati mcenje; adzakuseka pwepwete, nadzakunyoza muli zambiri m'menemo.

33. Udzadzala ndi kuledzera ndi cisoni, ndi cikho codabwitsa ndi ca cipasuko, ndi cikho ca mkuru wako Samariya.

34. Udzamwa ici ndi kugugudiza, ndi kuceceta-ceceta zibade zace, ndi kung'amba maere ako; pakuti ndacinena, ati Ambuye Yehova.

35. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza wandiiwala Ine, ndi kunditaya pambuyo pako, uzisenza iwenso coipa cako ndi zigololo zako.

36. Ndipo Yehova anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? uwafotokozere tsono zonyansa zao.

37. Pakuti anacita cigololo, ndi m'manja mwao muli mwazi, ndipo anacita cigololo ndi mafano ao, nawapititsiranso pamoto ana ao amuna amene anandibalira, kuti athedwe.

38. Anandicitiranso ici, anadetsa malo anga opatulika tsiku lomwelo naipsa masabata anga;

39. pakuti ataphera mafano ao, ana ao analowa tsiku lomwelo m'malo anga opatulika kuwadetsa; ndipo taona, anatero m'kati mwa nyumba yanga.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 23