Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 23:22-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Cifukwa cace, Oholiba, atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakuutsira mabwenzi ako amene moyo wako wakufidwa nao, ndi kukufikitsira iwowa pozungulira ponse atsutsane nawe,

23. a ku Babulo, ndi Akasidi, Pekodi, ndi Sowa, ndi Kowa, ndi Aasuri onse pamodzi nao, anyamata ofunika, ziwanga ndi akazembe onsewo, akalonga ndi mandoda onsewo, oyenda ndi akavalo.

24. Ndipo adzakudzera ndi zida, magareta a nkhondo, ndi magareta ena, pamodzi ndi msonkhano wa mitundu ya anthu; adzadziikira pozungulira pako ndi zikopa zocinjiriza ndi zisoti; ndipo ndidzawaika aweruze, nadzakuweruza monga mwa maweruzo ao.

25. Ndipo ndidzakuikira nsanje yanga, nadzakucitira mwaukali, iwowa adzakudula mphuno ndi makutu; ndi otsiriza ako adzagwa ndi lupanga, adzakucotsera ana ako amuna ndi akazi, ndi otsirizira ako adzatha ndi moto.

26. Adzakubvulanso zobvala zako, ndi kukucotsera zokometsera zako zokongola.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 23