Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 22:24-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Wobadwa ndi munthu iwe, nena ndi Yuda, Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, losabvumbwa mvula tsiku la ukalilo.

25. Pali ciwembu ca aneneri ace pakati pace, ngati mkango wobangula womwetula nyama, analusira miyoyo, alanda cuma ndi za mtengo wace, acurukitsa amasiye pakati pace.

26. Ansembe ace acitira coipa cilamulo canga, nadetsa zopatulika zanga, sasiyanitsa pakati pa zopatulika ndi zosapatulika, ndipo sazindikiritsa anthu pakati pa zodetsa ndi zoyera, nabisira masabata anga maso ao; ndipo Ine ndidetsedwa pakati pao.

27. Akalonga ace m'kati mwace akunga afisi akumwetula nyama, kukhetsa mwazi, kuononga miyoyo, kuti aone phindu lonyenga.

28. Ndipo aneneri ao anawamatira ndi dothi losapondeka, ndi kuonera zopanda pace, ndi kuwaombezera mabodza, ndi kuti, Atero Ambuye Yehova posanena Yehova.

29. Anthu a m'dziko anazunzazunza, nalandalanda mwaciwawa, napsinja ozunzika ndi aumphawi, nazunza mlendo wopanda cifukwa.

30. Ndipo ndinafunafuna munthu pakati pao wakumanganso linga, ndi kuimira dziko popasukira pamaso panga, kuti ndisaliononge; koma ndinapeza palibe.

31. Cifukwa cace ndinawatsanulira ukali wanga, ndawatha ndi moto wa kuzaza kwanga, njira yao yao ndinaibweza pa mutu pao, ati Ambuye Yehova.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 22