Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 20:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndipo ndinanena nao, Ali yense ataye zonyansa za pamaso pace, nimusadzidetsa ndi mafano a Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

8. Koma anapandukira Ine, osafuna kundimvera Ine, sanataya yense zonyansa pamaso pace, sanaleka mafano a Aigupto; pamenepo ndidati ndiwatsanulire ukali wanga, kuwakwaniritsira mkwiyo wanga m'dziko la Aigupto.

9. Koma ndinacicita cifukwa ca dzina langa, kuti lisadetsedwe pamaso pa amitundu amene anakhala pakati pao, amene pamaso pao ndinadzidziwitsa kwa iwo, pakuwaturutsa m'dziko la Aigupto.

10. Momwemo ndinaturuka nao m'dziko la Aigupto, ndi kulowa nao kucipululu.

11. Ndinawapatsanso malemba anga, ndi kuwadziwitsa maweruzo anga, ndiwo munthu akawacita adzakhala nao ndi moyo.

12. Ndipo ndinawapatsanso masabata anga akhale cizindikilo pakati pa Ine ndi iwo, kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova wakuwapatula.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 20