Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 20:27-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Cifukwa cace wobadwa ndi munthu iwe, lankhula ndi nyumba ya Israyeli, nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Mwa icinso atate anu anandicitira mwano pakundilakwira Ine.

28. Nditafika nao m'dzikolo ndinawakwezera dzanja langa kuwapatsa ilo, anapenya citunda ciri conse cacitali, ndi mtengo uli wonse wagudugudu, naphera pomwepo nsembe zao, napetekapo nsembe zao zondiputa, aponso anacita pfungo lao lokoma, nathiraponso nsembe zao zothira.

29. Pamenepo ndinanena nao, Msanje wotani uwu mumapitako? Momwemo dzina lace lichedwa Msanje, mpaka lero lino.

30. Cifukwa cace uziti kwa nyumba ya Israyeli, Atero Ambuye Yehova, Mudzidetsa kodi monga umo anacitira makolo anu? mucita cigololo kodi kutsata zonyansa zao?

31. ndipo popereka zopereka zanu popititsa ana anu pamoto, mudzidetsa kodi ndi mafano anu onse mpaka lero lino? ndipo kodi ndidzafunsidwa ndi inu, nyumba ya Israyeli? Pali Ine, ati Ambuye Yehova, sindidzafunsidwa ndi inu;

32. ndi ici cimauka mumtima mwanu sicidzacitika, umo mukuti, Tidzakhala ngati amitundu, ngati mabanja a m'maiko, kutumikira mtengo ndi mwala.

33. Pali Ine, ati Ambuye Yehova, zedi ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi ukali wotsanulidwa, ndidzakhala mfumu yanu.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 20